< Masalimo 83 >
1 Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
Canto. Salmo di Asaf. O Dio, non startene cheto; non rimaner muto ed inerte, o Dio!
2 Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
Poiché, ecco, i tuoi nemici si agitano rumorosamente, e quelli che t’odiano alzano il capo.
3 Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
Tramano astuti disegni contro il tuo popolo, e si concertano contro quelli che tu nascondi presso di te.
4 Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
Dicono: Venite, distruggiamoli come nazione, e il nome d’Israele non sia più ricordato.
5 Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
Poiché si son concertati con uno stesso sentimento, fanno un patto contro di te:
6 Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
le tende di Edom e gl’Ismaeliti; Moab e gli Hagareni;
7 Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
Ghebal, Ammon ed Amalek; la Filistia con gli abitanti di Tiro;
8 Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
anche l’Assiria s’è aggiunta a loro; prestano il loro braccio ai figliuoli di Lot. (Sela)
9 Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
Fa’ a loro come facesti a Midian, a Sisera, a Jabin presso al torrente di Chison,
10 Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
i quali furon distrutti a Endor, e serviron di letame alla terra.
11 Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
Rendi i loro capi simili ad Oreb e Zeeb, e tutti i loro principi simili a Zeba e Tsalmunna;
12 amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
poiché dicono: Impossessiamoci delle dimore di Dio.
13 Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
Dio mio, rendili simili al turbine, simili a stoppia dinanzi al vento.
14 Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
Come il fuoco brucia la foresta, e come la fiamma incendia i monti,
15 kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
così perseguitali con la tua tempesta, e spaventali col tuo uragano.
16 Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
Cuopri la loro faccia di vituperio, onde cerchino il tuo nome, o Eterno!
17 Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
Siano svergognati e costernati in perpetuo, siano confusi e periscano!
18 Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.
E conoscano che tu, il cui nome e l’Eterno, sei il solo Altissimo sopra tutta la terra.