< Masalimo 83 >

1 Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
Ein Psalmlied Assaphs. Gott, schweige doch nicht also und sei doch nicht so stille; Gott, halte doch nicht so inne!
2 Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
Denn siehe, deine Feinde toben, und die dich hassen, richten den Kopf auf.
3 Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
Sie machen listige Anschläge wider dein Volk und ratschlagen wider deine Verborgenen.
4 Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
Wohl her! sprechen sie, laßt uns sie ausrotten, daß sie kein Volk seien, daß des Namens Israel nicht mehr gedacht werde!
5 Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
Denn sie haben sich miteinander vereiniget und einen Bund wider dich gemacht:
6 Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
die Hütten der Edomiter und Ismaeliter, der Moabiter und Hagariter,
7 Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
der Gebaliter, Ammoniter und Amalekiter, die Philister, samt denen zu Tyrus;
8 Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
Assur hat sich auch zu ihnen geschlagen und helfen den Kindern Lot. (Sela)
9 Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
Tu ihnen wie den Midianitern, wie Sissera, wie Jabin am Bach Kison,
10 Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
die vertilget wurden bei Endor und wurden zu Kot auf Erden.
11 Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
Mache ihre Fürsten wie Oreb und Seeb, alle ihre Obersten wie Sebah und Zalmuna,
12 amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
die da sagen: Wir wollen die Häuser Gottes einnehmen.
13 Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
Gott, mache sie wie einen Wirbel, wie Stoppeln vor dem Winde!
14 Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
Wie ein Feuer den Wald verbrennet, und wie eine Flamme, die Berge anzündet,
15 kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
also verfolge sie mit deinem Wetter und erschrecke sie mit deinem Ungewitter.
16 Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
Mache ihr Angesicht voll Schande, daß sie nach deinem Namen fragen müssen.
17 Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
Schämen müssen sie sich und erschrecken immer mehr und mehr und zuschanden werden und umkommen.
18 Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

< Masalimo 83 >