< Masalimo 83 >

1 Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
Cantique. Psaume d’Assaph. O Dieu, n’arrête plus ton action, ne garde pas le silence, ne reste pas en repos, ô Tout-Puissant!
2 Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
Car voilà tes ennemis qui s’agitent en tumulte, et tes adversaires qui lèvent la tête.
3 Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
Contre ton peuple ils ourdissent des complots; ils se concertent contre ceux que tu protèges.
4 Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
Ils disent: "Allons, rayons-les du nombre des nations; que le nom d’Israël ne soit plus mentionné!"
5 Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
Car, d’un commun accord, ils prennent des résolutions, contre toi ils font un pacte:
6 Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
les tentes d’Edom et les Ismaélites, Moabites et Hagrites,
7 Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
Ghebal, Ammon et Amalec, les Philistins ainsi que les habitants de Tyr;
8 Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
Achour aussi se joint à eux; ils prêtent main-forte aux fils de Loth. (Sélah)
9 Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
Traite-les comme tu as traité Madian, Sisara et Jabin près du torrent de Kison,
10 Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
qui furent anéantis à Endor, couchés sur le sol comme du fumier.
11 Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
Rends leur noble pareille à Oreb et à Zeêb, et tous leurs princes, pareils à Zébah et Çalmouna,
12 amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
car ils ont dit: "Emparons-nous des demeures de Dieu."
13 Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
Mon Dieu, fais d’eux comme un tourbillon de poussière, comme du chaume emporté par le vent.
14 Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
De même que le feu dévore les forêts, que la flamme embrase les montagnes,
15 kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
ainsi pourchasse-les par ta tempête, jette-les dans une fuite éperdue par ton ouragan.
16 Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
Couvre leur visage d’opprobre, pour qu’ils recherchent ton nom, ô Eternel.
17 Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
Qu’ils soient confondus, terrifiés à jamais, saisis de honte et perdus.
18 Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.
Qu’ils reconnaissent ainsi que toi seul as nom Eternel, que tu es le Maître suprême de toute la terre.

< Masalimo 83 >