< Masalimo 83 >

1 Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
Cantique. Psaume d’Asaph. O Dieu, ne reste pas dans l’inaction; ne te tais pas et ne te repose pas, ô Dieu!
2 Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
Car voici que tes ennemis s’agitent bruyamment, ceux qui te haïssent lèvent la tête.
3 Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
Ils forment contre ton peuple un dessein perfide, ils conspirent contre ceux que tu protèges:
4 Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
« Venez, disent-ils, exterminons-les d’entre les nations, et qu’on ne prononce plus le nom d’Israël! »
5 Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
Ils se concertent tous d’un même cœur, contre toi ils forment une alliance,
6 Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
les tentes d’Edom et les Ismaélites, Moab et les Agaréniens,
7 Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
Gébal, Ammon et Amalec, les Philistins avec les habitants de Tyr;
8 Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
Assur aussi se joint à eux et prête son bras aux enfants de Lot. — Séla.
9 Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
Traite-les comme Madian, comme Sisara, comme Jabin au torrent de Cison.
10 Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
Ils ont été anéantis à Endor, ils ont servi d’engrais à la terre.
11 Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
Traite leurs chefs comme Oreb et Zeb, et tous leurs princes comme Zébée et Salmana.
12 amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
Car ils disent: « Emparons-nous des demeures de Dieu! »
13 Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
Mon Dieu, rends-les semblables au tourbillon, au chaume qu’emporte le vent!
14 Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
Comme le feu dévore la forêt, comme la flamme embrase les montagnes,
15 kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
ainsi poursuis-les dans ta tempête, épouvante-les dans ton ouragan.
16 Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
Couvre leurs faces d’ignominie, afin qu’ils cherchent ton nom, Yahweh.
17 Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
Qu’ils soient à jamais dans la confusion et l’épouvante, dans la honte et dans la ruine!
18 Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.
Qu’ils sachent que toi, — ton nom est Yahweh, — tu es seul le Très-Haut sur toute la terre!

< Masalimo 83 >