< Masalimo 83 >

1 Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
A Song; a Psalm of Asaph. O God, keep not silence; hold not thy peace, and be not still, O God:
2 Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
For behold, thine enemies make a tumult; and they that hate thee lift up the head.
3 Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
They take crafty counsel against thy people, and consult against thy hidden ones:
4 Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
They say, Come, and let us cut them off from being a nation, and let the name of Israel be mentioned no more.
5 Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
For they have consulted together with one heart: they have made an alliance together against thee.
6 Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
The tents of Edom and the Ishmaelites, Moab and the Hagarites;
7 Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
Gebal, and Ammon, and Amalek; Philistia, with the inhabitants of Tyre;
8 Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
Asshur also is joined with them: they are an arm to the sons of Lot. (Selah)
9 Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
Do unto them as to Midian; as to Sisera, as to Jabin, at the torrent of Kishon:
10 Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
Who were destroyed at Endor; they became as dung for the ground.
11 Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
Make their nobles as Oreb and as Zeeb; and all their chiefs as Zebah and as Zalmunna.
12 amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
For they have said, Let us take to ourselves God's dwelling-places in possession.
13 Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
O my God, make them like a whirling thing, like stubble before the wind.
14 Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
As fire burneth a forest, and as the flame setteth the mountains on fire,
15 kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
So pursue them with thy tempest, and terrify them with thy whirlwind.
16 Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
Fill their faces with shame, that they may seek thy name, O Jehovah.
17 Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
Let them be put to shame and be dismayed for ever, and let them be confounded and perish:
18 Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.
That they may know that thou alone, whose name is Jehovah, art the Most High over all the earth.

< Masalimo 83 >