< Masalimo 83 >
1 Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
Píseň a žalm Azafův. Bože, neodmlčujž se, nečiň se neslyše, aniž se upokojuj, ó Bože silný.
2 Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
Nebo aj, nepřátelé tvoji se bouří, a ti, kteříž tě v nenávisti mají, pozdvihují hlavy.
3 Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
Chytře tajné rady proti lidu tvému skládají, a radí se proti těm, kteréž ty skrýváš,
4 Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
Říkajíce: Poďte, a vyhlaďme je, ať nejsou národem, tak aby ani zpomínáno nebylo více jména Izraelova.
5 Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
Jednomyslněť se na tom spolu snesli, i smlouvou se proti tobě zavázali,
6 Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
Stánkové Idumejští a Izmaelitští, Moábští a Agarenští,
7 Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
Gebálští a Ammonitští, a Amalechitští, Filistinští s obyvateli Tyrskými.
8 Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
Ano i Assyrští spojili se s nimi, jsouce na ruku synům Lotovým. (Sélah)
9 Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
Učiniž jim jako Madianským, jako Zizarovi, a jako Jabínovi při potoku Císon,
10 Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
Kteříž jsou do konce vyhlazeni v Endor, a učiněni hnůj země.
11 Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
Nalož s nimi a s vůdci jejich jako s Gorébem, jako s Zébem, jako s Zebahem, a jako s Salmunou, se všemi knížaty jejich.
12 amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
Neboť jsou řekli: Uvažme se dědičně v příbytky Boží.
13 Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
Můj Bože, učiň to, ať jsou jako chumelice, a jako stéblo před větrem.
14 Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
Jakož oheň spaluje les, a jako plamen zapaluje hory,
15 kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
Tak ty je vichřicí svou stihej, a bouří svou ohrom je.
16 Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
Naplň tváře jejich zahanbením, tak aby hledali jména tvého, Hospodine.
17 Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
Nechať se hanbí a děsí na věčné časy, a ať potupu nesou a zahynou.
18 Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.
A tak ať poznají, že ty, kterýž sám jméno máš Hospodin, jsi nejvyšší nade vší zemí.