< Masalimo 83 >

1 Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
Асафова псаломска песен. Боже, недей мълча; Не премълчавай, нито бивай безмълвен, Боже;
2 Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
Защото, ето, враговете Ти правят размирие, И ненавистниците Ти са издигнали глава.
3 Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
Коварен съвет правят против Твоите люде, И се наговарят против скритите Твои.
4 Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
Рекох: Елате да ги изтребим, за да не са народ, И да се не споменава вече името на Израиля.
5 Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
Защото единодушно се съгласиха заедно, Направиха съюз против Тебе,
6 Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
Шатрите на Едом и исмаилите; Моав и агаряните.
7 Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
Гевал, Амон и Амалик, Филистимците с тирските жители;
8 Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
Още и Асирия се съедини с тях, Станаха помощници на Лотовите потомци. (Села)
9 Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
Стори им като на мадиамците, Като на Сисара, като на Якова при потока Кисон,
10 Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
Които загинаха в Ендор, Ставайки тор на земята.
11 Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
Направи благородните им като Орива и Зива, Дори всичките им първенци като Зевея и Салмана,
12 amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
Които рекоха: Да усвоим за себе си Божиите заселища.
13 Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
Боже мой, направи ги като въртящия се прах, Като плява пред вятъра.
14 Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
Както огънят изгаря лесовете, И както пламъкът запалва горите.
15 kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
Така ги прогони с урагана Си, И смути ги с бурята Си.
16 Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
Покрий лицата им с позор, За да потърсят Твоето име, Господи.
17 Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
Нека се посрамят и ужасят за винаги, Да! нека се смутят и погинат,
18 Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.
За да познаят, че Ти, Чието име е Иеова, Един си Всевишен над цялата земя.

< Masalimo 83 >