< Masalimo 82 >
1 Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
Ihubo lika-Asafi UNkulunkulu usesihlalweni emhlanganweni omkhulu; nguye owahlulelayo phakathi kwabo “nkulunkulu”:
2 “Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
“Koze kube nini livikela ababi na libonakala lithanda izigangi?
3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
Lamlelani ababuthakathaka lezintandane; melani amalungelo abayanga labahlukuluzwayo.
4 Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
Lamlelani ababuthakathaka labaswelayo; bephuleni esandleni sababi.
5 “Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
Onkulunkulu kabazi lutho, kabazwisisi lutho. Bayantula emnyameni; zonke izisekelo zomhlaba zixukuxiwe.
6 “Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
Ngathi, ‘Lingo “nkulunkulu”; lonke lingamadodana akhe oPhezukonke.’
7 Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
Kodwa lizakufa lingabantu nje; lizakuwa njengamanye amakhosi wonke.”
8 Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.
Phakama, Oh Nkulunkulu, yahlulela umhlaba, ngoba zonke izizwe ziyilifa lakho.