< Masalimo 82 >

1 Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
Mazmur Asaf. Allah memimpin sidang ilahi di surga, lalu Ia memberi keputusan-Nya:
2 “Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
"Jangan lagi mengadili dengan curang, dan jangan memihak kepada orang jahat.
3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
Belalah anak yatim dan orang lemah, berilah keadilan kepada orang miskin dan sengsara.
4 Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
Bebaskanlah orang yang lemah dan tak berdaya, luputkan mereka dari tangan orang jahat.
5 “Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
Kamu tak tahu apa-apa, bodoh dan sesat, karena kamu, tata tertib masyarakat berantakan.
6 “Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
Aku berkata bahwa kamu ilahi kamu sekalian anak-anak Allah Yang Mahatinggi.
7 Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
Tapi kamu akan mati seperti manusia, seperti setiap pembesar, kamu pun akan tewas."
8 Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.
Datanglah ya Allah, hakimilah dunia, sebab semua bangsa adalah milik-Mu.

< Masalimo 82 >