< Masalimo 82 >
1 Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
Ein Psalm Asaphs. Gott steht da in der Gottesversammlung,
2 “Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
»Wie lange noch wollt ihr ungerecht richten und Partei für die Gottlosen nehmen? (SELA)
3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
Schafft Recht dem Geringen und Verwaisten, dem Bedrückten und Dürftigen verhelft zum Recht!
4 Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
Rettet den Geringen und Armen, entreißt ihn der Hand der Gottlosen!«
5 “Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
»Doch sie sind ohne Einsicht und ohne Erkenntnis; in Finsternis gehn sie einher, mögen der Erde Pfeiler auch alle wanken.
6 “Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
Wohl hab’ ich selber gesagt, daß ihr Götter seid und Söhne des Höchsten allesamt;
7 Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
dennoch wie (gewöhnliche) Menschen sollt ihr sterben. und fallen wie irgendeiner der Fürsten.«
8 Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.
Erhebe dich, Gott, richte die Erde! Denn du bist der Erbherr über alle Völker.