< Masalimo 82 >

1 Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
Psaume d’Asaph.
2 “Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
Jusques à quand jugerez-vous selon l’iniquité, et ferez-vous acception de la personne des pécheurs?
3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
Jugez pour l’indigent et le pupille: faites justice à l’humble et au pauvre.
4 Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
Délivrez le pauvre, et arrachez l’indigent de la main du pécheur.
5 “Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
Ils n’ont pas su, et ils n’ont pas compris; ils marchent dans les ténèbres; tous les fondements de la terre seront ébranlés.
6 “Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
Moi j’ai dit: Vous êtes des dieux, et fils du Très-Haut, tous.
7 Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
Mais vous mourrez comme des hommes; et comme l’un des princes, vous tomberez.
8 Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.
Levez-vous, ô Dieu, jugez la terre; parce que vous hériterez parmi toutes les nations.

< Masalimo 82 >