< Masalimo 82 >
1 Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
Un psaume d'Asaph. Dieu préside la grande assemblée. Il juge parmi les dieux.
2 “Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
« Jusqu'à quand jugerez-vous injustement, et faire preuve de partialité envers les méchants? (Selah)
3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
« Défendez le faible, le pauvre et l'orphelin. Maintenir les droits des pauvres et des opprimés.
4 Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
Secourir les faibles et les nécessiteux. Délivre-les de la main des méchants. »
5 “Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
Ils ne savent pas, ils ne comprennent pas non plus. Ils vont et viennent dans l'obscurité. Toutes les fondations de la terre sont ébranlées.
6 “Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
J'ai dit: « Vous êtes des dieux, vous êtes tous des fils du Très-Haut.
7 Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
Néanmoins, vous mourrez comme des hommes, et tomber comme un des chefs. »
8 Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.
Lève-toi, Dieu, juge la terre, car vous héritez de toutes les nations.