< Masalimo 82 >
1 Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
A Psalm of Asaph. God standeth in the congregation of God; he judgeth among the gods.
2 “Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
How long will ye judge unjustly, and respect the persons of the wicked? (Selah)
3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
Judge the poor and fatherless: do justice to the afflicted and destitute.
4 Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
Rescue the poor and needy: deliver them out of the hand of the wicked.
5 “Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
They know not, neither do they understand; they walk to and fro in darkness: all the foundations of the earth are moved.
6 “Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
I said, Ye are gods, and all of you sons of the Most High.
7 Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
Nevertheless ye shall die like men, and fall like one of the princes.
8 Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.
Arise, O God, judge the earth: for thou shalt inherit all the nations.