< Masalimo 82 >

1 Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
“A psalm of Asaph.” God standeth in God's assembly, He judgeth in the midst of the gods.
2 “Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
“How long will ye judge unjustly, And favor the cause of the wicked? (Pause)
3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
Defend the poor and the fatherless; Do justice to the wretched and the needy!
4 Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
Deliver the poor and the destitute; Save them from the hand of the wicked!
5 “Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
They are without knowledge and without understanding; They walk in darkness: Therefore all the foundations of the land are shaken.
6 “Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
I have said, Ye are gods, And all of you children of the Most High;
7 Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
But ye shall die like men, And fall like the rest of the princes.”
8 Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.
Arise, O God! judge the earth! For all the nations are thy possession.

< Masalimo 82 >