< Masalimo 82 >
1 Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
A Psalm for Asaph. God stands in the assembly of gods; and in the midst [of them] will judge gods.
2 “Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
How long will you judge unrighteously, and accept the persons of sinners? (Pause)
3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
Judge the orphan and poor: do justice to the low and needy.
4 Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
Rescue the needy, and deliver the poor out of the hand of the sinner.
5 “Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
They know not, nor understand; they walk on in darkness: all the foundations of the earth shall be shaken.
6 “Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
I have said, You are gods; and all [of you] children of the Most High.
7 Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
But you die as men, and fall as one of the princes.
8 Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.
Arise, O God, judge the earth: for you shall inherit all nations.