< Masalimo 82 >

1 Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
A psalm of Asaph. God stands in the midst of his great assembly to judge among the gods.
2 “Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
How long will you make unfair judgments and show favoritism to the wicked? (Selah)
3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
Defend the poor and orphans; support the rights of those who are oppressed and suffering.
4 Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
Rescue the poor and those unable to help themselves; save them from the clutches of evil people.
5 “Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
They don't have any wisdom; they live in the dark; the foundations of the earth are shaken.
6 “Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
I say, “You are gods; all of you are children of the Most High.
7 Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
But you will die like any human being, you will fall like any other leader.”
8 Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.
Stand up, Lord, and judge the earth, for all the nations belong to you.

< Masalimo 82 >