< Masalimo 82 >

1 Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
Gud staar i Guds Menighed; han dømmer midt iblandt Guder.
2 “Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
Hvor længe ville I dømme Uret og anse de ugudeliges Personer? (Sela)
3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
Skaffer den ringe og den faderløse Ret; hjælper den elendige og den arme til Retfærdighed!
4 Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
Redder den ringe og den fattige; udfrier ham af de ugudeliges Haand!
5 “Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
De skønne ikke og forstaa ikke, de vandre i Mørke; alle Jordens Grundpiller ryste.
6 “Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
Jeg har sagt: I ere Guder, og I ere alle den Højestes Sønner.
7 Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
Men I skulle dø som Mennesker, og som en af Fyrsterne skulle I falde.
8 Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.
Gud! gør dig rede, døm Jorden; thi du skal tage Arv iblandt alle Hedninger.

< Masalimo 82 >