< Masalimo 81 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
Haz un canto a Dios, nuestra fortaleza: lanza un alegre clamor al Dios de Jacob!
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Canten al son del pandero, con él arpa y él salterio.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Toquen el cuerno en el tiempo de la luna nueva, en la luna llena, en nuestro día de fiesta santa:
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
Porque esta es la ley de Israel, y la ley del Dios de Jacob.
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
Se lo dio a José como testigo cuando salió a la tierra de Egipto; entonces las palabras de una extraña lengua sonaban en mis oídos.
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
Bajé el peso de su espalda; sus manos se hicieron libres de las cestas.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
Tú soltaste un grito en tu tribulación, y yo te hice libre; Te di una respuesta en el lugar secreto del trueno; Te puse a prueba en las aguas de Meribah. (Selah)
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
Escucha, pueblo mío, y te daré mi palabra, oh Israel, si solo haces lo que digo.
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
No habrá ningún dios extraño entre ustedes; no debes rendir culto a ningún otro dios.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
Yo soy el Señor tu Dios, que te subío de la tierra de Egipto; abre tu boca, para que yo te dé de comer.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
Pero mi pueblo no escuchó mi voz; Israel no quiso obedecerme, nada que ver conmigo.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
Así que los entregué a los deseos de sus corazones; para que puedan ir tras sus malvados propósitos.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
Si tan solo mi gente me escuchara, caminando en mis caminos!
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
Yo rápidamente vencería a sus enemigos: mi mano se volvería contra aquellos que hacen la guerra contra ellos.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
Los que odiaban al Señor serían quebrantados, y su destrucción sería eterna.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
Yo les daría el mejor grano por comida; estarías lleno de miel de la roca.

< Masalimo 81 >