< Masalimo 81 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
Al Músico principal: sobre Gittith: Salmo de Asaph. CANTAD á Dios, fortaleza nuestra: al Dios de Jacob celebrad con júbilo.
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Tomad la canción, y tañed el adufe, el arpa deliciosa con el salterio.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Tocad la trompeta en la nueva luna, en el día señalado, en el día de nuestra solemnidad.
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
Porque estatuto es de Israel, ordenanza del Dios de Jacob.
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
Por testimonio en José lo ha constituído, cuando salió por la tierra de Egipto; [donde] oí lenguaje que no entendía.
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
Aparté su hombro de debajo de la carga; sus manos se quitaron de vasijas de barro.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
En la calamidad clamaste, y yo te libré: te respondí en el secreto del trueno; te probé sobre las aguas de Meriba. (Selah)
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
Oye, pueblo mío, y te protestaré. Israel, si me oyeres,
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
No habrá en ti dios ajeno, ni te encorvarás á dios extraño.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
Yo soy Jehová tu Dios, que te hice subir de la tierra de Egipto: ensancha tu boca, y henchirla he.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
Mas mi pueblo no oyó mi voz, é Israel no me quiso á mí.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
Dejélos por tanto á la dureza de su corazón: caminaron en sus consejos.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
¡Oh, si me hubiera oído mi pueblo, si en mis caminos hubiera Israel andado!
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
En una nada habría yo derribado sus enemigos, y vuelto mi mano sobre sus adversarios.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
Los aborrecedores de Jehová se le hubieran sometido; y el tiempo de ellos fuera para siempre.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
[Y Dios] lo hubiera mantenido de grosura de trigo: y de miel de la piedra te hubiera saciado.