< Masalimo 81 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
Načelniku godbe pri Gitaji, pesem Asafu. Pojte Bogu, móči naši, vpijte Bogu Jakobovemu.
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Primite psalmovanje in vzemite boben, strune prijetne in brenklje.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Trobite o mlaji, o vseh stalnih praznikih, o godovih naših.
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
Ker ustanovljeno je v Izraelu, postava od Boga Jakobovega,
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
Kateri jo je za pričanje postavil v Jožefu, ko je šel proti deželi Egiptovski, kjer sem slišal govor neznan;
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
"Odtegnil sem", pravi, od bremena ramo njegovo; roke njegove ločile so se od čebriča.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
Ko si vpil v oni stiski, rešil sem te, uslišal sem te v gromovem zakotji; izkušal sem te do vodâ Meribskih.
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
Poslušaj, ljudstvo moje, in spričeval ti bodem, o Izrael, ako me bodeš poslušal.
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
Ako ne bode v tebi boga mogočnega tujega, in se ne bodeš klanjal bogu mogočnemu tujerodnemu.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
Jaz sem Gospod, Bog tvoj, ki sem dal, da si prišel gor iz dežele Egiptovske; razširi usta svoja in napolnim jih.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
Ali ljudstvo moje ni poslušalo glasu mojega, in Izrael mi ni bil pokoren.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
Zatorej sem jih izpustil, da naj hodijo po srca svojega volji, govoreč: Gredó naj sè svojimi krivimi naklepi.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
O ko bi me bilo poslušalo ljudstvo moje, ko bi bili Izraelci hodili po mojih potih!
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
Kar mahoma bi bil potlačil njih neprijatelje, ko bi bil v njih sovražnike obrnil roko svojo.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
Sovražniki Gospodovi bi se bili lažnjivo vdali njemu, in njih čas bi bil vekomaj.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
Dà, živil bi ga bil z maščobo pšenično, tudi z medom iz skale bi te bil sitil.