< Masalimo 81 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
Glasno prepevajte Bogu, naši môči, naredite radosten glas Jakobovemu Bogu.
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Vzemite psalm in prinesite sèm tamburin, prijetno harfo s plunko.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Trobite na šofar ob mlaju, ob določenem času na naš slovesni praznični dan.
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
Kajti to je bil zakon za Izraela in postava Jakobovega Boga.
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
To je odredil v Jožefu za pričevanje, ko je šel ven skozi egiptovsko deželo, kjer sem slišal jezik, ki ga nisem razumel:
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
»Njegovo ramo sem odstranil od bremena, njegove roke so bile osvobojene pred lonci.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
Ti kličeš v stiski in jaz sem te osvobodil, odgovoril sem ti na skrivnem kraju groma. Jaz sem te preizkusil pri vodah Meríbe. (Sela)
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
Poslušaj, oh moje ljudstvo, pričeval ti bom, oh Izrael, če bi mi hotel prisluhniti.
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
V tebi naj ne bo tujega boga niti ne boš oboževal nobenega tujega boga.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
Jaz sem Gospod, tvoj Bog, ki te je privedel iz egiptovske dežele. Široko odpri svoja usta in napolnil jih bom.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
Toda moje ljudstvo noče prisluhniti mojemu glasu in Izrael noče ničesar od mene.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
Tako sem jih izročil njihovim lastnim srčnim željam in živeli so po svojih lastnih nasvetih.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
Oh, da bi mi moje ljudstvo prisluhnilo in bi Izrael hodil po mojih poteh!
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
Kmalu bi podjarmil njihove sovražnike in svojo roko obrnil zoper njihove nasprotnike.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
Gospodovi sovražniki bi se morali podvreči pod njega, pa bi se njihov čas ohranil na veke.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
Hranil bi jih tudi z najodličnejšo pšenico in z medom iz skale bi te nasitil.«

< Masalimo 81 >