< Masalimo 81 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
Psalmus Asaph, in finem, pro torcularibus, quinta sabbati. Exultate Deo adiutori nostro: iubilate Deo Iacob.
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Sumite psalmum, et date tympanum: psalterium iucundum cum cithara.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Buccinate in Neomenia tuba, in insigni die sollemnitatis vestrae:
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
Quia praeceptum in Israel est: et iudicium Deo Iacob.
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
Testimonium in Ioseph posuit illud, cum exiret de Terra Aegypti: linguam, quam non noverat, audivit.
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
Divertit ab oneribus dorsum eius: manus eius in cophino servierunt.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
In tribulatione invocasti me, et liberavi te: exaudivi te in abscondito tempestatis: probavi te apud aquam contradictionis.
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
Audi populus meus, et contestabor te: Israel si audieris me,
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
non erit in te deus recens, neque adorabis deum alienum.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
Ego enim sum Dominus Deus tuus, qui eduxi te de terra Aegypti: dilata os tuum, et implebo illud.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
Et non audivit populus meus vocem meam: et Israel non intendit mihi.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
Et dimisi eos secundum desideria cordis eorum, ibunt in adinventionibus suis.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
Si populus meus audisset me: Israel si in viis meis ambulasset:
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
Pro nihilo forsitan inimicos eorum humiliassem: et super tribulantes eos misissem manum meam.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
Inimici Domini mentiti sunt ei: et erit tempus eorum in saecula.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
Et cibavit eos ex adipe frumenti: et de petra, melle saturavit eos.

< Masalimo 81 >