< Masalimo 81 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
Pour le chef musicien. Sur un instrument de Gath. Par Asaph. Chantez à voix haute à Dieu, notre force! Poussez un cri de joie vers le Dieu de Jacob!
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Élevez une chanson, et apportez ici le tambourin, la lyre agréable avec la harpe.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Sonnez la trompette à la nouvelle lune, à la pleine lune, le jour de notre fête.
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
Car c'est une loi pour Israël, une ordonnance du Dieu de Jacob.
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
Il l'a établi en Joseph comme une alliance, quand il a traversé le pays d'Égypte, J'ai entendu une langue que je ne connaissais pas.
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
« J'ai enlevé son épaule du fardeau. Ses mains ont été libérées du panier.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
Tu as appelé dans la détresse, et je t'ai délivré. Je t'ai répondu dans le lieu secret du tonnerre. Je t'ai testé aux eaux de Meribah. (Sélah)
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
« Écoute, mon peuple, et je te rendrai témoignage, Israël, si tu m'écoutais!
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
Il n'y aura pas de dieu étranger chez vous, et vous n'adorerez aucun dieu étranger.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
Je suis Yahvé, votre Dieu, qui vous a fait sortir du pays d'Égypte. Ouvrez grand votre bouche, et je la remplirai.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
Mais mon peuple n'a pas écouté ma voix. Israël ne voulait pas de moi.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
Je les ai donc laissés aller selon l'obstination de leur cœur, pour qu'ils suivent leurs propres conseils.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
Oh, que mon peuple m'écoute! qu'Israël marche dans mes voies!
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
J'allais bientôt soumettre leurs ennemis, et je tournerai ma main contre leurs adversaires.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
Les ennemis de Yahvé s'effaceront devant lui, et leur punition durerait éternellement.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
Mais il les aurait aussi nourris avec le meilleur du blé. Je te rassasierai avec le miel du rocher. »

< Masalimo 81 >