< Masalimo 81 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
Sing aloud to God, our strength! Make a joyful shout to the God of Jacob [Supplanter]!
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Raise a song, and bring here the tambourine, the pleasant lyre with the harp.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Blow the shofar ·ram horn· at the New Moon, at the full moon, on our feast day.
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
For it is a statute for Israel [God prevails], an judgement of the God of Jacob [Supplanter].
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
He appointed it in Joseph [May he add] for a testimony, when he went out over the land of Egypt [Abode of slavery], I sh'ma ·heard obeyed· a language that I didn’t know.
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
“I removed his shoulder from the burden. His hands were freed from the basket.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
You called in trouble, and I delivered you. I answered you in the secret place of thunder. I tested you at the waters of Meribah [Quarreling].” (Selah) ·contemplation with musical interlude·.
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
“Sh'ma ·Hear obey·, my people, and I will testify to you, Israel [God prevails], if you would listen to me!
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
There shall be no strange deity in you, neither shall you hawa ·bow low, prostrate· to worship any foreign deity.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
I am Adonai, your God, who brought you up out of the land of Egypt [Abode of slavery]. Open your mouth wide, and I will fill it.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
But my people didn’t sh'ma ·hear obey· my voice. Israel [God prevails] desired none of me.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
So I let them go after the stubbornness of their hearts, that they might walk in their own counsels.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
Oh that my people would sh'ma ·hear obey· me, that Israel [God prevails] would walk in my ways!
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
I would soon subdue their enemies, and turn my hand against their adversaries.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
The haters of Adonai would cringe before him, and their punishment would last forever.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
But he would have also fed them with the finest of the wheat. I will satisfy you with honey out of the rock.”

< Masalimo 81 >