< Masalimo 81 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
[For the Chief Musician. On an instrument of Gath. By Asaph.] Sing aloud to God, our strength. Make a joyful shout to the God of Jacob.
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Raise a song, and bring here the tambourine, the pleasant lyre with the harp.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Blow the trumpet at the New Moon, at the full moon, on our feast day.
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
For it is a statute for Israel, an ordinance of the God of Jacob.
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
He appointed it in Joseph for a testimony, when he went out over the land of Egypt, I heard a language that I did not know.
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
"I removed his shoulder from the burden. His hands were freed from the basket.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
You called in trouble, and I delivered you. I answered you in the secret place of thunder. I tested you at the waters of Meribah." (Selah)
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
"Hear, my people, and I will testify to you, Israel, if you would listen to me.
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
There shall be no strange god in you, neither shall you worship any foreign god.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
I am the LORD, your God, who brought you up out of the land of Egypt. Open your mouth wide, and I will fill it.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
But my people did not listen to my voice. Israel desired none of me.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
So I let them go after the stubbornness of their hearts, that they might walk in their own counsels.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
Oh that my people would listen to me, that Israel would walk in my ways.
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
I would soon subdue their enemies, and turn my hand against their adversaries.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
The haters of the LORD would cringe before him, and their punishment would last forever.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
And he would have fed him with the finest wheat, and satisfied you with honey from the rock."

< Masalimo 81 >