< Masalimo 81 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
Unto the end, for the winepresses, a psalm for Asaph himself. Rejoice to God our helper: sing aloud to the God of Jacob.
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Take a psalm, and bring hither the timbrel: the pleasant psaltery with the harp.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Blow up the trumpet on the new moon, on the noted day of your solemnity.
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
For it is a commandment in Israel, and a judgment to the God of Jacob.
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
He ordained it for a testimony in Joseph, when he came out of the land of Egypt: he heard a tongue which he knew not.
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
He removed his back from the burdens: his hands had served in baskets.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
Thou calledst upon me in affliction, and I delivered thee: I heard thee in the secret place of tempest: I proved thee at the waters of contradiction.
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
Hear, O my people, and I will testify to thee: O Israel, if thou wilt hearken to me,
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
There shall be no new god in thee: neither shalt thou adore a strange god.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
For I am the Lord thy God, who brought thee out of the land of Egypt: open thy mouth wide, and I will fill it.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
But my people heard not my voice: and Israel hearkened not to me.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
So I let them go according to the desires of their heart: they shall walk in their own inventions.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
If my people had heard me: if Israel had walked in my ways:
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
I should soon have humbled their enemies, and laid my hand on them that troubled them.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
The enemies of the Lord have lied to him: and their time shall be for ever.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
And he fed them with the fat of wheat, and filled them with honey out of the rock.

< Masalimo 81 >