< Masalimo 81 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
To the chief Musician. Upon the Gittith. [A Psalm] of Asaph. Sing ye joyously unto God our strength, shout aloud unto the God of Jacob;
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Raise a song, and sound the tambour, the pleasant harp with the lute.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Blow the trumpet at the new moon, at the set time, on our feast day:
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
For this is a statute for Israel, an ordinance of the God of Jacob;
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
He ordained it in Joseph [for] a testimony, when he went forth over the land of Egypt, [where] I heard a language that I knew not.
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
I removed his shoulder from the burden; his hands were freed from the basket.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
Thou calledst in trouble, and I delivered thee; I answered thee in the secret place of thunder; I proved thee at the waters of Meribah. (Selah)
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
Hear, my people, and I will testify unto thee; O Israel, if thou wouldest hearken unto me!
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
There shall no strange god be in thee, neither shalt thou worship any foreign god.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
I am Jehovah thy God, that brought thee up out of the land of Egypt: open thy mouth wide, and I will fill it.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
But my people hearkened not to my voice, and Israel would none of me.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
So I gave them up unto their own hearts' stubbornness: they walked after their own counsels.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
Oh that my people had hearkened unto me, that Israel had walked in my ways!
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
I would soon have subdued their enemies, and turned my hand against their adversaries.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
The haters of Jehovah would have come cringing unto him; but their time would have been for ever.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
And he would have fed them with the finest of wheat; yea, with honey out of the rock would I have satisfied thee.

< Masalimo 81 >