< Masalimo 81 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
Přednímu z kantorů na gittit, Azafovi. Plésejte Bohu, síle naší, prokřikujte Bohu Jákobovu.
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Vezměte žaltář, přidejte buben, harfu libou a loutnu.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Trubte trubou na novměsíce, v uložený čas, v den slavnosti naší.
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
Nebo toť jest ustavení v Izraeli, řád Boha Jákobova.
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
Na svědectví v Jozefovi vyzdvihl jej, když byl vyšel proti zemi Egyptské, kdež jsme jazyk neznámý slýchati musili.
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
Osvobodil jsem, dí Bůh, od břemene rameno jeho, a ruce jeho nádob zednických zproštěny byly.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
V ssoužení tom, když jsi volal, vytrhl jsem tě, vyslyšel jsem tě z skrýše hromu, zkušoval jsem tě při vodách sváru. (Sélah)
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
Řeklť jsem: Slyš, lide můj, a osvědčím se tobě, ó Izraeli, budeš-li mne poslouchati,
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
A nebude-li mezi vámi Boha jiného, a nebudeš-li se klaněti bohu cizímu.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
Já jsem Hospodin Bůh tvůj, kterýž jsem tě vyvedl z země Egyptské, otevři jen ústa svá, a naplnímť je.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
Ale neuposlechl lid můj hlasu mého, a Izrael nepřestal na mně,
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
A protož pustil jsem je v žádost srdce jejich, i chodili po radách svých.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
Ó byť mne byl lid můj poslouchal, a Izrael po cestách mých chodil,
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
Tudíž bych já byl nepřátely jejich snížil, a na protivníky jejich obrátil ruku svou.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
A ti, kteříž v nenávisti mají Hospodina, úlisně by se jim poddávati musili, i byl by čas jejich až na věky.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
A krmil bych je byl jádrem pšenice, a medem z skály sytil bych je.

< Masalimo 81 >