< Masalimo 81 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
Zborovođi. Po napjevu “Tijesci”. Asafov. Kliknite Bogu, našoj jakosti, kličite Bogu Jakovljevu!
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Nek' zazvuče žice, nek' se čuje bubanj, svirajte u milozvučnu harfu s citarom!
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Zatrubite u rog za mlađaka, za uštapa, na svetkovinu našu!
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
Jer to je propis Izraelu, zapovijed Boga Jakovljeva.
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
Takav je zakon dao Josipu kad je izlazio iz zemlje Egipta.
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
Šapat tajnovit čuh: “Oslobodih od tereta rame njegovo, ruke su mu slobodne od košare.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
U tjeskobi si zavapio i ja te izbavih; iz gromovna oblaka odgovorih tebi, iskušah te kod voda meripskih.
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
Slušaj, puče moj, i ja ću te opomenuti: o, da me poslušaš, Izraele!
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
Nek' ne bude u tebe drugog boga i ne klanjaj se bogu tuđem!
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
Ja sam Jahve, Bog tvoj koji te izvedoh iz Egipta: otvori svoja usta da ih napunim!”
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
“Ali moj narod ne slušaše glasa moga, Izrael me ne posluša.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
Zato ga pustih okorjelom srcu njegovu: neka hodi kako mu se hoće!
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
O, kad bi me narod moj slušao, kad bi Izrael putovima mojim hodio,
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
brzo bih pokorio dušmane njegove, ruku bih svoju okrenuo na protivnike njegove.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
Oni što ga sada mrze dodvarali bi mu se i njihov bi udes bio zapečaćen zauvijek.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
A svoj narod hranio bih pšenicom najboljom i sitio ga medom iz pećine.