< Masalimo 81 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
亞薩的詩,交與伶長。用迦特樂器。 你們當向上帝-我們的力量大聲歡呼, 向雅各的上帝發聲歡樂!
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
唱起詩歌,打手鼓, 彈美琴與瑟。
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
當在月朔並月望- 我們過節的日期吹角,
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
因這是為以色列定的律例, 是雅各上帝的典章。
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
他去攻擊埃及地的時候, 在約瑟中間立此為證。 我在那裏聽見我所不明白的言語:
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
上帝說:我使你的肩得脫重擔, 你的手放下筐子。
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
你在急難中呼求,我就搭救你; 我在雷的隱密處應允你, 在米利巴水那裏試驗你。 (細拉)
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
我的民哪,你當聽,我要勸戒你; 以色列啊,甚願你肯聽從我。
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
在你當中,不可有別的神; 外邦的神,你也不可下拜。
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
我是耶和華-你的上帝, 曾把你從埃及地領上來; 你要大大張口,我就給你充滿。
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
無奈,我的民不聽我的聲音; 以色列全不理我。
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
我便任憑他們心裏剛硬, 隨自己的計謀而行。
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
甚願我的民肯聽從我, 以色列肯行我的道,
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
我便速速治服他們的仇敵, 反手攻擊他們的敵人。
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
恨耶和華的人必來投降, 但他的百姓必永久長存。
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
他也必拿上好的麥子給他們吃, 又拿從磐石出的蜂蜜叫他們飽足。