< Masalimo 80 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
Пастире Израиљев, чуј! Који водиш синове Јосифове као овце, који седиш на херувимима, јави се!
2 kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
Пред Јефремом и Венијамином и Манасијом пробуди крепост своју, и ходи да нам помогнеш.
3 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Боже! Поврати нас, нека засја лице Твоје да се спасемо!
4 Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
Господе, Боже над војскама! Докле ћеш се гневити кад Те моли народ Твој?
5 Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
Храниш их хлебом сузним, и појиш их сузама троструком мером.
6 Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
Учинио си да се око нас свађају суседи наши, и непријатељи се наши смеју међу собом.
7 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Боже над војскама! Поврати нас, нека засја лице Твоје да се спасемо!
8 Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
Из Мисира си пренео чокот, изагнао народе, и посадио га.
9 Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
Окрчио си за њ, и он пусти жиле, и заузе сву земљу.
10 Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
Горе се покрише његовим сеном, и лозе су му као кедри Божији.
11 Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
Пустио је лозе своје до мора и огранке своје до реке.
12 Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
Зашто си му развалио ограду, да га кида ко год прође?
13 Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
Горски вепар подгриза га, и пољска звер једе га.
14 Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
Боже над војскама! Обрати се, погледај с неба и види, и обиђи виноград овај,
15 muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
Сад овај, који је посадила десница Твоја, и сина ког си укрепио себи!
16 Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
Попаљен је огњем, исечен, од страшног погледа Твог пропаде.
17 Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
Нека буде рука Твоја над човеком деснице Твоје, над сином човечијим ког си утврдио себи!
18 Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
И нећемо одступити од Тебе, оживи нас, и име Твоје призиваћемо.
19 Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Господе, Боже над војскама! Поврати нас, нека засја лице Твоје, да се спасемо!

< Masalimo 80 >