< Masalimo 80 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
Psalmus, in finem, pro iis, qui commutabuntur, testimonium Asaph. Qui regis Israel, intende: qui deducis velut ovem Ioseph. Qui sedes super cherubim, manifestare
2 kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
coram Ephraim, Beniamin, et Manasse. Excita potentiam tuam, et veni, ut salvos facias nos.
3 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Deus converte nos: et ostende faciem tuam, et salvi erimus.
4 Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
Domine Deus virtutum, quousque irasceris super orationem servi tui?
5 Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
Cibabis nos pane lacrymarum: et potum dabis nobis in lacrymis in mensura?
6 Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
Posuisti nos in contradictionem vicinis nostris: et inimici nostri subsannaverunt nos.
7 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Deus virtutum converte nos: et ostende faciem tuam: et salvi erimus.
8 Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
Vineam de Aegypto transtulisti: eiecisti Gentes, et plantasti eam.
9 Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
Dux itineris fuisti in conspectu eius: plantasti radices eius, et implevit terram.
10 Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
Operuit montes umbra eius: et arbusta eius cedros Dei.
11 Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
Extendit palmites suos usque ad mare: et usque ad flumen propagines eius.
12 Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
Ut quid destruxisti maceriam eius: et vindemiant eam omnes, qui praetergrediuntur viam?
13 Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
Exterminavit eam aper de silva: et singularis ferus depastus est eam.
14 Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
Deus virtutum convertere: respice de caelo, et vide, et visita vineam istam.
15 muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
Et perfice eam, quam plantavit dextera tua: et super filium hominis, quem confirmasti tibi.
16 Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
Incensa igni, et suffossa ab increpatione vultus tui peribunt.
17 Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
Fiat manus tua super virum dexterae tuae: et super filium hominis, quem confirmasti tibi.
18 Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
Et non discedimus a te, vivificabis nos: et nomen tuum invocabimus.
19 Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Domine Deus virtutum converte nos: et ostende faciem tuam, et salvi erimus.

< Masalimo 80 >