< Masalimo 80 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
Pour la fin, pour ceux qui seront changés, témoignage d’Asaph, psaume. Vous qui gouvernez Israël, soyez attentif: vous qui conduisez, comme une brebis, Joseph. Vous qui êtes assis sur les Chérubins, manifestez-vous
2 kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
Devant Ephraïm, Benjamin et Manassé.
3 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Ô Dieu, convertissez-nous, et montrez votre face, et nous serons sauvés.
4 Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
Seigneur, Dieu des armées, jusques à quand serez-vous irrité au sujet de la prière de votre serviteur?
5 Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
Jusques à quand nous nourrirez-vous d’un pain de larmes, et nous donnerez-vous à boire des larmes dans une mesure?
6 Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
Vous nous avez posés comme un objet de contradiction à nos voisins; et nos ennemis nous ont insultés.
7 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Dieu des armées, convertissez-nous, et montrez votre face, et nous serons sauvés.
8 Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
Vous avez transporté de l’Égypte une vigne, vous avez chassé des nations, et vous l’avez plantée.
9 Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
Vous avez été un guide de route devant elle: vous avez planté ses racines, et elle a rempli la terre.
10 Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
Son ombre a couvert les montagnes, et ses rameaux les cèdres de Dieu.
11 Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
Elle a étendu ses branches jusqu’à la mer, et ses rameaux jusqu’au fleuve.
12 Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
Pourquoi donc avez-vous détruit son mur de clôture, et pourquoi la vendangent-ils, tous ceux qui passent dans le chemin?
13 Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
Un sanglier de forêt l’a entièrement dévastée; et une bête sauvage l’a broutée.
14 Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
Dieu des armées, revenez, regardez du haut du ciel et voyez, et visitez cette vigne.
15 muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
Faites-la prospérer, celle que votre droite à plantée, et portez vos regards sur le fils de l’homme que vous avez établi fermement pour vous.
16 Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
Elle a été brûlée par le feu et déchaussée; par la réprimande de votre visage ils périront.
17 Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
Que votre main repose sur l’homme de votre droite, et sur le fils de l’homme que vous avez établi fermement pour vous.
18 Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
Et nous ne nous éloignerons plus de vous; vous nous rendrez la vie, et nous invoquerons votre nom.
19 Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Seigneur, Dieu des armées, convertissez-nous; et montrez votre face, et nous serons sauvés.

< Masalimo 80 >