< Masalimo 80 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
Au maître-chantre. — Sur «Les lis rendent témoignage». — Psaume d'Asaph. Prête l'oreille, berger d'Israël! Toi qui conduis Joseph comme un troupeau. Toi dont le trône est au-dessus des chérubins, Fais rayonner ta splendeur!
2 kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
Devant Éphraïm, Benjamin et Manassé, réveille ta puissance, Et viens nous sauver.
3 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Dieu, relève-nous; Fais resplendir ta face, et nous serons sauvés!
4 Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
Éternel, Dieu des armées, Jusques à quand répondras-tu par la colère A la prière de ton peuple?
5 Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
Tu nous fais manger un pain trempé de nos pleurs; Tu nous abreuves sans mesure de nos larmes.
6 Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
Tu nous livres aux outrages de nos voisins, Et nos ennemis se raillent de nous.
7 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Dieu des armées, relève-nous; Fais resplendir ta face, et nous serons sauves!
8 Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
Tu tiras de l'Egypte une vigne, Et, pour la planter, tu chassas des nations.
9 Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
Tu déblayas le sol devant elle; Elle jeta ses racines et couvrit la terre.
10 Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
Les montagnes furent couvertes de son ombre. Et ses rameaux ombrageaient les cèdres de Dieu.
11 Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
Elle étendait ses pampres jusqu'à la mer, Et ses rejetons jusqu'au fleuve.,
12 Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
Pourquoi as-tu rompu ses clôtures. En sorte que tous les passants la dépouillent,
13 Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
Que le sanglier des forêts la dévaste. Et que les bêtes des champs en font leur pâture?
14 Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
Dieu des armées, reviens! Regarde des cieux, vois, et visite cette vigne!
15 muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
Protège le cep que ta main droite a planté, Et le rejeton que tu t'es choisi.
16 Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
Ta vigne est brûlée; elle est saccagée; Tout périt devant l'éclat de ton courroux.
17 Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
Étends ta protection sur le peuple Que ta main droite a choisi, Sur les fils des hommes que tu as élus!
18 Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
Alors, nous ne nous détournerons plus de toi. Rends-nous la vie, et nous invoquerons ton nom.
19 Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Éternel, Dieu des armées, relève-nous! Fais resplendir ta face, et nous serons sauvés!

< Masalimo 80 >