< Masalimo 80 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
Au chef des chantres. Sur les Chochanim, Edouth. Psaume d’Assaph. Pasteur d’Israël, prête l’oreille, toi qui mènes Joseph comme un troupeau! Révèle-toi dans ta splendeur, toi qui trônes sur les Chérubins!
2 kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
Aux regards d’Ephraïm, Benjamin et Manassé, déploie ta puissance, et marche à notre secours!
3 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
O Dieu, régénère-nous, fais luire ta face et nous serons sauvés!
4 Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
Eternel, Dieu-Cebaot! Jusques à quand accueilleras-tu avec colère la prière de ton peuple?
5 Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
Tu leur fais manger un pain trempé de pleurs, tu les abreuves d’un déluge de larmes.
6 Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
Tu fais de nous un brandon de discorde pour nos voisins, et nos ennemis se livrent à leurs moqueries.
7 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
O Dieu-Cebaot, régénère-nous, fais luire ta face et nous serons sauvés!
8 Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
Tu as fait émigrer une vigne de l’Egypte, et expulsé des nations pour la replanter.
9 Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
Tu as fait place nette devant elle; aussi elle jeta de profondes racines, et s’étendit sur le pays.
10 Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
Les montagnes furent couvertes de son ombrage, ses branches égalèrent les cèdres de Dieu.
11 Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
Elle poussa ses sarments jusqu’à la mer, jusqu’au Fleuve ses rejetons.
12 Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
Pourquoi as-tu démoli ses clôtures, si bien que tous les passants la dépouillent,
13 Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
que le sanglier de la forêt la mutile, et qu’elle sert de pâture à ce qui se meut dans les champs?
14 Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
O Dieu-Cébaot! Reviens de grâce! Du haut du Ciel regarde et vois; prends sous ta protection cette vigne,
15 muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
ces ceps que ta droite a mis en terre, cette plantation que tu avais voulue si vigoureuse.
16 Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
La voilà consumée par le feu, mise en pièces: sous la colère menaçante de ta face, tout périt!
17 Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
Oh! que ta protection s’étende sur l’homme élu par ta droite, sur le fils de l’homme que tu avais rendu fort en ton honneur!
18 Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
Nous ne nous éloignerons plus de toi: ranime notre vie, et nous invoquerons ton nom.
19 Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
O Eternel, Dieu-Cebaot, régénère-nous, fais luire ta face et nous serons sauvés!

< Masalimo 80 >