< Masalimo 80 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
To the choirmaster to Shoshannim eduth of Asaph a psalm. O shepherd of Israel - give ear! O [you who] lead like flock Joseph O [you who] sit the cherubim shine forth!
2 kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
Before Ephraim - and Benjamin and Manasseh stir up! might your and come! for salvation of us.
3 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
O God restore us and make shine face your so let us be delivered.
4 Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
O Yahweh God of hosts until when? have you smoked at [the] prayer of people your.
5 Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
You have fed them bread of tear[s] and you have made drink them tears a third of a measure.
6 Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
You make us a contention to neighbors our and enemies our they mock themselves.
7 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
O God of hosts restore us and make shine face your so let us be delivered.
8 Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
A vine from Egypt you uprooted you drove out nations and you planted it.
9 Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
You made clear before it and it took root roots its and it filled [the] land.
10 Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
They were covered mountains shade its and branches its [the] cedars of God.
11 Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
It stretched out branch[es] its to [the] sea and to [the] river young shoots its.
12 Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
Why? have you broken down walls its and they have plucked it all [those who] pass by of [the] road.
13 Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
It eats away it wild boar from [the] forest and moving creature[s] of [the] field it grazes on it.
14 Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
O God of hosts return please pay attention from heaven and see and attend to vine this.
15 muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
And [the] root which it planted right [hand] your and on [the] son [whom] you made strong for yourself.
16 Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
[it is] burned With fire [it is] cut down from [the] rebuke of face your they will perish.
17 Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
May it be hand your on [the] man of right [hand] your on [the] son of humankind [whom] you have made strong for yourself.
18 Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
And not we will turn back from you you will give life us and on name your we will call.
19 Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
O Yahweh God of hosts restore us make shine face your so let us be delivered.

< Masalimo 80 >