< Masalimo 80 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
To the Chief Musician. For "the Lilies of Testimony." Asaph’s. A Melody. O Shepherd of Israel, give ear, Thou who leddest forth Joseph like a rock, Thou who art throned on the cherubim, appear!
2 kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
Before Ephraim and Benjamin and Manasseh, stir up thy strength, And come! to our salvation.
3 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
O God, bring us back, And light up thy face, That we may be saved.
4 Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
O Yahweh, God of hosts! How long hast thou been wroth with the prayer of thy people?
5 Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
Thou hast fed them with the food of tears, And hast caused them to drink the water of weeping in threefold abundance.
6 Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
Thou dost make us an object of contention to our neighbours, And, our foes, find mockery for themselves.
7 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
O God of hosts, bring us back, And light up thy face, That we may be saved.
8 Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
A vine out of Egypt, thou didst remove, Thou didst cast out nations, and plant it;
9 Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
Thou didst make a clear space before it, So it rooted well its roots, and filled up the land;
10 Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
Covered were the mountains with its shade, And, with its boughs, the mighty cedars.
11 Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
It thrust forth its branches as far as the sea, —And, unto the River, its shoots.
12 Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
Wherefore hast thou broken down its fences, So that all who pass along the way, pluck its fruit?
13 Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
The boar out of the forest, browseth upon it, And, the wild beast of the field, pastureth thereon.
14 Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
O God of hosts, return, we pray thee, —Look down out of the heavens, and see, And inspect this vine:
15 muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
Yea the stock which thy right hand planted, Even upon the son thou didst secure for thyself.
16 Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
To be burned with fire, it is cut down, —At the rebuke of thy countenance, they will perish.
17 Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
Let thy hand be, Upon the Man of thy right hand, Upon the Son of Man thou didst secure for thyself;
18 Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
So will we not draw back from thee, Thou wilt bring us to life, And, on thy Name, will we call.
19 Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
O Yahweh, God of hosts! bring us back, Light up thy face, That we may be saved.

< Masalimo 80 >