< Masalimo 80 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
Unto the end, for them that shall he changed, a testimony for Asaph, a psalm. Give ear, O thou that rulest Israel: thou that leadest Joseph like a sheep. Thou that sittest upon the cherubims, shine forth
2 kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
Before Ephraim, Benjamin, and Manasses. Stir up thy might, and come to save us.
3 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Convert us, O God: and shew us thy face, and we shall be saved.
4 Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
O Lord God of hosts, how long wilt thou be angry against the prayer of thy servant?
5 Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
How long wilt thou feed us with the bread of tears: and give us for our drink tears in measure?
6 Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
Thou hast made us to be a contradiction to our neighbours: and our enemies have scoffed at us.
7 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
O God of hosts, convert us: and shew thy face, and we shall be saved.
8 Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
Thou hast brought a vineyard out of Egypt: thou hast cast cut the Gentiles and planted it.
9 Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
Thou wast the guide of its journey in its sight: thou plantedst the roots thereof, and it filled the land.
10 Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
The shadow of it covered the hills: and the branches thereof the cedars of God.
11 Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
It stretched forth its branches unto the sea, and its boughs unto the river.
12 Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
Why hast thou broken down the hedge thereof, so that all they who pass by the way do pluck it?
13 Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
The boar out of the wood hath laid it waste: and a singular wild beast hath devoured it.
14 Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
Turn again, O God of hosts, look down from heaven, and see, and visit this vineyard:
15 muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
And perfect the same which thy right hand hath planted: and upon the son of man whom thou hast confirmed for thyself.
16 Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
Things set on fire and dug down shall perish at the rebuke of thy countenance.
17 Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
Let thy hand be upon the man of thy right hand: and upon the son of man whom thou hast confirmed for thyself.
18 Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
And we depart not from thee, thou shalt quicken us: and we will call upon thy name.
19 Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
O Lord God of hosts, convert us: and shew thy face, and we shall be saved.

< Masalimo 80 >