< Masalimo 80 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
To the chief Musician. On Shoshannim-Eduth. Of Asaph. A Psalm. Give ear, O Shepherd of Israel, thou that leadest Joseph like a flock; thou that sittest [between] the cherubim, shine forth.
2 kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
Before Ephraim and Benjamin and Manasseh, stir up thy strength, and come to our deliverance.
3 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
O God, restore us; and cause thy face to shine, and we shall be saved.
4 Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
Jehovah, God of hosts, how long will thine anger smoke against the prayer of thy people?
5 Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
Thou hast fed them with the bread of tears, and given them tears to drink in large measure:
6 Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
Thou hast made us a strife unto our neighbours, and our enemies mock among themselves.
7 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Restore us, O God of hosts; and cause thy face to shine, and we shall be saved.
8 Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
Thou broughtest a vine out of Egypt; thou didst cast out the nations, and plant it:
9 Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
Thou preparedst space before it, and it took deep root, and filled the land;
10 Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
The mountains were covered with its shadow, and the branches thereof were [like] cedars of God;
11 Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
It sent out its boughs unto the sea, and its shoots unto the river.
12 Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
Why hast thou broken down its fences, so that all who pass by the way do pluck it?
13 Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
The boar out of the forest doth waste it, and the beast of the field doth feed off it.
14 Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
O God of hosts, return, we beseech thee; look down from the heavens, and behold, and visit this vine;
15 muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
Even the stock which thy right hand hath planted, and the young plant thou madest strong for thyself.
16 Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
It is burned with fire, it is cut down; they perish at the rebuke of thy countenance.
17 Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
Let thy hand be upon the man of thy right hand, upon the son of man whom thou hast made strong for thyself.
18 Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
So will we not go back from thee. Revive us, and we will call upon thy name.
19 Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Restore us, O Jehovah, God of hosts; cause thy face to shine, and we shall be saved.

< Masalimo 80 >