< Masalimo 80 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
За първия певец, по като кринове е заявлението. Асафов псалом. Послушай, Пастирю Израилев, Който водиш като стадо Иосифа; Ти, който обитаваш между херувимите, възсияй.
2 kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
Пред Ефрема Вениамина и Манасия раздвижи силата Си, И дойди да ни спасиш.
3 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Възвърни ни, Боже, и осияй с лицато Си; И ще се спасим.
4 Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
Господи Боже на Силите До кога ще пазиш гняв против молитвите на людете Си?
5 Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
Даваш им да ядат хляб със сълзи. И поиш ги изобилно със сълзи.
6 Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
Направил си ни предмет, на разпра между съседите ни; И неприятелите ни се смеят помежду си.
7 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Възвърни ни Боже на Силите, Осияй с лицето Си и ще се спасим,
8 Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
Пренесъл си лоза из Египет. И като си изгонил народите нея си насадил.
9 Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
Приготвил си място пред нея; И тя е пуснала дълбоко корени, и е изпълнила земята.
10 Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
Покриха се бърдата със сянката й; И клоновете й станаха като изящните кедри,
11 Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
Простря клончетата до морето. И ластарите си до Евфрат.
12 Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
Защо си съборил плетищата й, Та я берат всички, които минават през пътя?
13 Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
Запустява я глиган от гората, И полските зверове я пояждат.
14 Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
Обърни се, молим Ти се, Боже на Силите, Погледни от небето, и виж, и посети тая лоза,
15 muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
И защити това, което е насадила Твоята десница, И отрасъла
16 Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
Тя биде изгорена с огън; отсечена биде; Погиват при заплахата на лицето Ти.
17 Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
Нека бъде ръката Ти върху мъжа на Твоята десница Върху човешкия син, когото си направил силен за Себе Си.
18 Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
Така ние не ще се отклоним от Тебе; Съживи ни и ще призовем Твоето име.
19 Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Възвърни ни, Господи Боже на Силите; Осияй с лицето Си, и ще се спасим.

< Masalimo 80 >