< Masalimo 8 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
Керівнику хору. Виконання в стилі ґіттіт. Псалом Давидів. Господи, Володарю наш, яке величне ім’я Твоє усюди на землі! Ти підніс велич Свою понад небеса.
2 Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
Із вуст малих дітей і немовлят Ти влаштував твердиню проти супротивників Твоїх, щоб змусити замовкнути ворога й месника.
3 Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
Коли дивлюсь я на небеса Твої, творіння Твоїх пальців, на місяць і зорі, що Ти встановив їх,
4 munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
[то роздумую: ] «Хто така людина, що Ти пам’ятаєш про неї, і [хто] син людський, що Ти турбуєшся про нього?»
5 Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
Лише трохи применшив Ти його перед Богом і славою та величчю коронував його.
6 Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
Ти поставив його панувати над творіннями Твоїх рук, усе підкорив йому під ноги:
7 nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
усю дрібну худобу й волів, а також польових звірів,
8 mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
птахів небесних і риб морських, [усе живе], що проходить стежками моря.
9 Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!
Господи, Володарю наш, яке величне ім’я Твоє усюди на землі!

< Masalimo 8 >