< Masalimo 8 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
Müzik şefi için - Gittit üzerine - Davut'un mezmuru Ey Egemenimiz RAB, Ne yüce adın var yeryüzünün tümünde! Gökyüzünü görkeminle kapladın.
2 Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
Çocukların, hatta emziktekilerin sesiyle Set çektin hasımlarına, Düşmanı, öç alanı yok etmek için.
3 Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
Seyrederken ellerinin eseri olan gökleri, Oraya koyduğun ayı ve yıldızları,
4 munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
Soruyorum kendi kendime: “İnsan ne ki, onu anasın, Ya da insanoğlu ne ki, ona ilgi gösteresin?”
5 Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
Nerdeyse bir tanrı yaptın onu, Başına yücelik ve onur tacını koydun.
6 Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
Ellerinin yapıtları üzerine onu egemen kıldın, Her şeyi ayaklarının altına serdin;
7 nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
Davarları, sığırları, Yabanıl hayvanları,
8 mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
Gökteki kuşları, denizdeki balıkları, Denizde kıpırdaşan bütün canlıları.
9 Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!
Ey Egemenimiz RAB, Ne yüce adın var yeryüzünün tümünde!

< Masalimo 8 >