< Masalimo 8 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
En Psalm Davids, till att föresjunga på Gittith. Herre, vår Herre, huru härligit är ditt Namn i all land, der man tackar dig i himmelen.
2 Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
Utaf unga barnas och spenabarnas mun hafver du ena magt upprättat, för dina ovänners skull; att du skall nederlägga ovännen, och den hämndgiruga.
3 Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
Ty jag skall se himlarna, dins fingers verk; månan och stjernorna, som du beredt hafver.
4 munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
Hvad är menniskan, att du tänker på henne; eller menniskones son, att du låter dig vårda om honom?
5 Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
Du skall låta honom en liten tid af Gudi öfvergifven varda; men med äro och härlighet skall du kröna honom.
6 Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
Du skall göra honom till en herra öfver dina händers verk; all ting hafver du under hans fötter lagt:
7 nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
Får och fä alltsamman; vilddjuren också dertill;
8 mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
Foglarna under himmelen, och fiskarna i hafvet, och hvad i hafvena går.
9 Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!
Herre, vår Herre, huru härligit är ditt Namn i all land.