< Masalimo 8 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
Para el director del coro. Sobre el Gitit. Un salmo de David. ¡Señor, nuestro Señor, tu majestoso nombre llena toda la tierra! Tu majestad es más grande que los cielos,
2 Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
y lo cantan las voces de los niños. Tu fuerza sobrepasa a tus oponentes, y silencias al enemigo y al vengador.
3 Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
Cuando contemplo los cielos que hicieron tus manos, la luna y las estrellas que en él pusiste,
4 munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
¿Qué son los seres humanos para que pienses en ellos? ¿Qué somos las personas para que cuides de nosotros?
5 Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
Los creaste un poco menores que Dios, coronándoles de gloria y majestad.
6 Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
Los pusiste a cargo de toda tu creación, dándoles autoridad sobre todo:
7 nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
sobre las ovejas, sobre el ganado, sobre los animales del campo,
8 mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
sobre las aves del cielo, y los peces del mar, así como sobre todo lo que nada en el océano.
9 Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!
Señor, nuestro Señor, tu majestuoso nombre llena toda la tierra.

< Masalimo 8 >