< Masalimo 8 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
Ó Senhor, nosso Senhor, quão admiravel é o teu nome em toda a terra, pois pozeste a tua gloria sobre os céus!
2 Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
Tu ordenaste força da bocca das creanças e dos que mamam, por causa dos teus inimigos, para fazer calar ao inimigo e ao vingador.
3 Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
Quando vejo os teus céus, obra dos teus dedos, a lua e as estrellas que preparaste;
4 munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
Que é o homem mortal para que te lembres d'elle? e o filho do homem, para que o visites?
5 Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
Pois pouco menor o fizeste do que os anjos, e de gloria e de honra o coroaste.
6 Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
Fazes com que elle tenha dominio sobre as obras das tuas mãos; tudo pozeste debaixo de seus pés:
7 nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
Todas as ovelhas e bois, assim como os animaes do campo,
8 mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
As aves dos céus, e os peixes do mar, e tudo o que passa pelas veredas dos mares.
9 Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!
Ó Senhor, nosso Senhor, quão admiravel é o teu nome sobre toda a terra!