< Masalimo 8 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
Til sangmesteren, efter Gittit; en salme av David. Herre, vår Herre, hvor herlig ditt navn er over all jorden, du som har utbredt din prakt over himmelen!
2 Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
Av barns og diebarns munn har du grunnfestet en makt for dine motstanderes skyld, for å stoppe munnen på fienden og den hevngjerrige.
3 Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
Når jeg ser din himmel, dine fingrers gjerning, månen og stjernene, som du har gjort,
4 munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
hvad er da et menneske, at du kommer ham i hu, og et menneskebarn, at du ser til ham!
5 Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
Og du gjorde ham lite ringere enn Gud, og med ære og herlighet kronte du ham.
6 Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
Du gjorde ham til hersker over dine henders gjerninger, alt la du under hans føtter,
7 nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
får og okser, alle tilsammen, ja også markens dyr,
8 mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
himmelens fugler og havets fisker, alt som ferdes på havenes stier.
9 Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!
Herre, vår Herre, hvor herlig ditt navn er over all jorden!