< Masalimo 8 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
Nkosi, Nkosi yethu, lilenkazimulo kangakanani ibizo lakho emhlabeni wonke! Omise ubukhosi bakho ngaphezu kwamazulu.
2 Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
Emlonyeni wezingane lowabamunyayo umisile amandla ngenxa yezitha zakho, ukuze uthulise isitha lomphindiseli.
3 Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
Lapho ngikhangela amazulu akho, umsebenzi weminwe yakho, inyanga lenkanyezi owazimisayo,
4 munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
uyini umuntu ukuthi umkhumbule, lendodana yomuntu ukuthi uyihambele?
5 Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
Kanti wamenza waba ngaphansi kancinyane kulengilosi, wamethwesa umqhele wobukhosi lodumo.
6 Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
Wamenza wabusa phezu kwemisebenzi yezandla zakho, konke wakubeka ngaphansi kwenyawo zakhe,
7 nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
izimvu lenkabi zonke, kanye lezinyamazana zeganga,
8 mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
inyoni zamazulu, lezinhlanzi zolwandle, okudlula ezindleleni zenlwandle.
9 Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!
Nkosi, Nkosi yethu, lilenkazimulo kangakani ibizo lakho emhlabeni wonke!

< Masalimo 8 >