< Masalimo 8 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
Au maître-chantre. — Sur la Guittith. — Psaume de David. Éternel, notre Seigneur, Que ton nom est magnifique sur toute la terre! Ta majesté s'élève au-dessus des cieux.
2 Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
De la bouche des petits enfants, Même de ceux qu'on allaite, Tu tires ta louange pour confondre tes adversaires, Pour réduire au silence l'ennemi et le rebelle.
3 Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
Quand je contemple les cieux, oeuvre de tes mains, La lune et les étoiles que tu y as placées,
4 munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
Je dis: Qu'est-ce que l'homme, pour que tu te souviennes de lui? Et le fils de l'homme, pour que tu prennes garde à lui?
5 Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
Tu l'as créé à peine inférieur à un dieu! Tu l'as couronné de gloire et de magnificence.
6 Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
Tu lui as donné l'empire sur les oeuvres de tes mains; Tu as mis toutes choses sous ses pieds:
7 nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
Les brebis comme les boeufs, Et même les bêtes sauvages,
8 mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
Les oiseaux du ciel et les poissons de l'océan, Tout ce qui parcourt les sentiers des mers.
9 Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!
Éternel, notre Seigneur, Que ton nom est magnifique sur toute la terre!

< Masalimo 8 >