< Masalimo 8 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
To the ouercomere, for pressours, the salm of Dauid. Lord, thou art oure Lord; thi name is ful wonderful in al erthe. For thi greet doyng is reisid, aboue heuenes.
2 Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
Of the mouth of yonge children, not spekynge and soukynge mylk, thou madist perfitli heriyng, for thin enemyes; that thou destrie the enemy and avengere.
3 Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
For Y schal se thin heuenes, the werkis of thi fyngris; the moone and sterris, whiche thou hast foundid.
4 munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
What is a man, that thou art myndeful of hym; ethir the sone of a virgyn, for thou visitist hym?
5 Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
Thou hast maad hym a litil lesse than aungels; thou hast corouned hym with glorie and onour,
6 Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
and hast ordeyned hym aboue the werkis of thin hondis.
7 nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
Thou hast maad suget alle thingis vndur hise feet; alle scheep and oxis, ferthermore and the beestis of the feeld;
8 mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
the briddis of the eir, and the fischis of the see; that passen bi the pathis of the see.
9 Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!
Lord, `thou art oure Lord; thi name `is wondurful in al erthe.