< Masalimo 8 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
to/for to conduct upon [the] Gittith melody to/for David LORD lord our what? great name your in/on/with all [the] land: country/planet which to give: put [emph?] splendor your upon [the] heaven
2 Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
from lip infant and to suckle to found strength because to vex you to/for to cease enemy and to avenge
3 Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
for to see: see heaven your deed: work finger your moon and star which to establish: make
4 munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
what? human for to remember him and son: child man for to reckon: visit him
5 Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
and to lack him little from God and glory and glory to crown him
6 Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
to rule him in/on/with deed: work hand your all to set: put underneath: under foot his
7 nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
sheep and cattle all their and also animal field
8 mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
bird heaven and fish [the] sea to pass way sea
9 Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!
LORD lord our what? great name your in/on/with all [the] land: country/planet

< Masalimo 8 >